Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 26:1-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Koma Yobu anayankha, nati,

2. Wamthandiza bwanji wopanda mphamvu,Kulipulumutsa dzanja losalimba!

3. Wampangira bwanji wopanda nzeruyu!Ndi kudziwitsa nzeru zeni zeni mocurukal

4. Wafotokozera yani mau?Ndi mzimu wa yani unaturuka mwa iwe?

5. Adafawo anjenjemeraPansi pa madzi ndi zokhalamo,

6. Kumanda kuli padagu pamaso pace,Ndi kucionongeko kusowa cophimbako,

7. Ayala kumpoto popanda kanthu, Nalenjeka dziko pacabe.

8. Amanga madzi m'mitambo yace yocindikira;Ndi mtambo sung'ambika pansi pace,

9. Acingira pa mpando wace wacifumu,Nayalapo mtambo wace.

10. Analembera madziwo malire,Mpaka polekeza kuunika ndi mdima.

11. Mizati ya thambo injenjemera,Ndi kudabwa pa kudzudzula kwace.

Werengani mutu wathunthu Yobu 26