Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 24:9-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Akwatula wamasiye kubere,Natenga cikole cobvala ca osauka;

10. Momwemo ayenda amarisece opanda cobvala,Nasenza mtolo wa dzinthu ali ndi njala.

11. M'kati mwa malinga a iwo aja ayenga mafuta;Aponda mphesa moponderamo, namva ludzu.

12. M'mudzi waukuru anthu abuula alinkufa;Ndi moyo wa iwo olasidwa upfuula;Koma Mulungu sasamalira coipaco.

13. Iwo ndiwo amene apikisana nako kuunika,Sadziwa njira zace,Sasunga mayendedwe ace.

14. Kukaca auka wambanda, napha wosauka ndi waumphawi;Ndi usiku asanduka mbala.

15. Ndipo diso la wacigololo liyombekezera cisisira,Ndi kuti, Palibe diso lidzandiona;Nabvala cophimba pankhope pace.

16. Kuli mdima aboola nyumba,Usana adzitsekera,Osadziwa kuunika.

17. Pakuti iwo onse auyesa m'mawa mthunzi wa imfa;Pakuti adziwa zoopsa za mthunzi wa imfa.

18. Atengedwa ngati coyandama pamadzi;Gawo lao litembereredwa padziko;Sadzalunjikanso njira ya minda yamphesa.

19. Cirala ndi dzuwa zitha madzi a cipale cofewa,Momwemo manda acita nao ocimwa.

20. M'mimba mudzamuiwala; mphutsi zidzamudya mokondwera.Sadzamkumbukilanso;Ndipo cosalungama cidzatyoledwa ngati mtengo.

Werengani mutu wathunthu Yobu 24