Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 24:1-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Wamphamvuyonse alekeranji kuikiratu nyengo?Ndi iwo omdziwa alekeranji kudziwa masiku ace?

2. Alipo akusendeza malire;Alanda gulu la zoweta, nazidyetsa.

3. Akankhizira kwao buru wa amasiye,Atenga ng'ombe ya mfedwa ikhale cikole.

4. Apambukitsa aumphawi m'njira;Osauka a padziko abisala pamodzi.

5. Taonani, ngati mbidzi za m'cipululuAturukira ku nchito zao, nalawirira nkufuna cakudya;Cipululu ciwaonetsera cakudya ca ana ao.

6. Atema dzinthu zao m'munda;Natola khunkha m'munda wampesa wa woipa.

Werengani mutu wathunthu Yobu 24