Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 23:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Koma Yobu anayankha, nati,

2. Lero lomwe kudandaula kwanga kumawawa;Kulanga kwanga kuposa kubuula kwanga m'kulemera kwace.

3. Ha! ndikadadziwa kumene ndikampeza Mulungu,Kuti ndifike ku mpando wace!

4. Ndikadalongosola mlandu wanga pamaso pace,Ndikadadzaza m'kamwa mwanga ndi matsutsano.

5. Ndikadadziwa mau akadandiyankha ine,Ndikadazindikira cimene akadanena nane.

Werengani mutu wathunthu Yobu 23