2. Zoonadi, ali nane ondiseka;Ndi diso langa liri cipenyere m'kundiwindula kwao.
3. Mupatse cigwiriro tsono, mundikhalire cikole Inu nokha kwanu;Ndani adzapangana nane kundilipirira?
4. Pakuti mwabisira mtima wao nzeru;Cifukwa cace simudzawakuza.
5. Iye wakupereka mabwenzi ace kuukapolo,M'maso mwa ana ace mudzada.
6. Anandiyesanso nthanthi za anthu;Ndipo ndakhala ngati munthu womthira malobvu pankhope pace.