Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 17:11-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Masiku anga apitirira, zolingirira zanga zaduka,Zace zace zomwe za mtima wanga.

12. Zisanduliza usiku ukhale usana;Kuunika kuyandikana ndi mdima.

13. Ndikayembekezera kumanda kukhale nyumba yanga;Ndikayala pogona panga mumdima.

14. Ndikati kwa dzenje, Ndiwe atate wanga;Kwa mphutsi, Ndiwe mai wanga ndi mlongo wanga;

15. Ciri kuti ciyembekezo canga?Inde, ciyembekezo canga adzaciona ndani?

16. Cidzatsikira ku mipingiridzo ya kumanda,Pamene tipumulira pamodzi kupfumbi.

Werengani mutu wathunthu Yobu 17