Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 16:5-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Koma ndikadakulimbikitsani ndi m'kamwa mwanga,Ndi citonthozo ca milomo yanga cikadatsitsa cisoni canu.

6. Cinkana ndinena cisoni canga sicitsika;Ndipo ndikaleka, cindicokera nciani?

7. Koma tsopano wandilemetsa Iye;Mwapasula msonkhano wanga wonse.

8. Kundigwira kwanu, ndiko umboni wonditsutsa,Kuonda kwanga kundiukira, kucita umboni pamaso panga.

9. Iye ananding'amba m'kundida kwace, nakwiya nane,Anandikukutira mano;Mdani wanga ananditong'olera maso ace.

10. Iwo anandiyasamira pakamwa pao;Anandiomba pama ndi kunditonza;Asonkhana pamodzi kunditsutsa.

11. Mulungu andipereka kwa osalungama,Nandiponya m'manja a oipa.

12. Ndinali mkupuma, koma anandityola;Inde anandigwira pakhosi, nandiphwanya;Anandiimika ndikhale candamali.

Werengani mutu wathunthu Yobu 16