Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 14:9-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Koma pa mnunkho wa madzi udzaphuka,Nudzaswa nthambi ngati womera.

10. Koma munthu akufa atacita liondeondeInde, munthu apereka mzimu wace, ndipo ali kuti?

11. Madzi acoka m'nyanja,Ndi mtsinje ukuphwa, nuuma;

12. Momwemo munthu agona pansi, osaukanso;Kufikira miyamba kulibe, sadzaukanso,Kapena kuutsidwa pa tulo tace.

13. Ha! mukadandibisa kumanda,Mukadandisunga m'tseri, mpaka wapita mkwiyo wanu.Mukadandiikira nthawi, ndi kundikumbukira.

14. Atafa munthu, adzakhalanso ndi moyo kodi?Ndikadayembekeza masiku onse a nkhondo yanga,Mpaka kwafika kusandulika kwanga,

15. Mukadaitana, ndipo ndikadakuyankhani;Mukadakhumba nchito ya manja anu.

Werengani mutu wathunthu Yobu 14