Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 14:17-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Colakwa canga caikidwa m'thumba lokomedwa cizindikilo;Ndipo mumanga pamodzi mphulupulu zanga.

18. Ndipo zoonadi, likagwa phiri, latha;Ndi thanthwe lisunthika m'malo mwace;

19. Madzi anyenya miyala;Zosefukira zao zikokolola pfumbi la nthaka;Ndipo muononga ciyembekezo ca munthu.

20. Mumlaka cilakire, napita iye;Musintha nkhope yace, mumuuza acoke.

21. Ana ace aona ulemu osadziwa iye;Napeputsidwa, koma osazindikira za iwo.

22. Koma thupi lace limuwawira yekha,Ndi mtima wace umliritsa yekha.

Werengani mutu wathunthu Yobu 14