Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 7:8-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Pakuti mutu wa Aramu ndi Damasiko, ndi mutu wa Damasiko ndi Rezini, zisadapite zaka makumi asanu ndi limodzi mphambu zisanu Efraimu adzatyokatyoka, sadzakhalanso mtundu wa anthu;

9. ndipo mutu wa Efraimu ndi Samariya, ndi mutu wa Samariya ndi mwana wa Remaliya, mukapanda kukhulupirira ndithu simudzakhazikika.

10. Ndipo Yehova ananenanso kwa Ahazi nati,

11. Udzipemphere wekha cizindikilo ca kwa Yehova Mulungu wako; pempha cam'mwakuya, kapena cam'mwamba.

12. Koma Ahazi anati, Sindipemphai ngakhale kumyesa Yehova.

13. Ndipo iye anati, Mverani inu tsopano, inu a nyumba ya Davide; kodi ndi kanthu kakang'ono kwa inu kutopetsa anthu, kuti inu mutopetsa Mulungu wanga?

14. Cifukwa cace Ambuye mwini yekha adzakupatsani inu cizindikilo; taonani namwali adzaima, nadzabala mwana wamwamuna, nadzamucha dzina lace Imanueli.

15. Iye adzadya mafuta ndi uci, pamene adziwa kukana coipa ndi kusankha cabwino.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 7