Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 7:6-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Tiyeni, tikwere, timenyane ndi Yuda, timbvute; tiyeni, tidzigumulire mpata, pamenepo tikhazike mfumu pakati pace, ngakhale mwana wamwamuna wa Tabeeli;

7. atero Ambuye Yehova, Upo wao sudzaimai, sudzacitidwa.

8. Pakuti mutu wa Aramu ndi Damasiko, ndi mutu wa Damasiko ndi Rezini, zisadapite zaka makumi asanu ndi limodzi mphambu zisanu Efraimu adzatyokatyoka, sadzakhalanso mtundu wa anthu;

9. ndipo mutu wa Efraimu ndi Samariya, ndi mutu wa Samariya ndi mwana wa Remaliya, mukapanda kukhulupirira ndithu simudzakhazikika.

10. Ndipo Yehova ananenanso kwa Ahazi nati,

11. Udzipemphere wekha cizindikilo ca kwa Yehova Mulungu wako; pempha cam'mwakuya, kapena cam'mwamba.

12. Koma Ahazi anati, Sindipemphai ngakhale kumyesa Yehova.

13. Ndipo iye anati, Mverani inu tsopano, inu a nyumba ya Davide; kodi ndi kanthu kakang'ono kwa inu kutopetsa anthu, kuti inu mutopetsa Mulungu wanga?

14. Cifukwa cace Ambuye mwini yekha adzakupatsani inu cizindikilo; taonani namwali adzaima, nadzabala mwana wamwamuna, nadzamucha dzina lace Imanueli.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 7