Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 7:21-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Ndipo padzakhala tsiku limenelo, kuti munthu adzaweta ng'ombe yaikazi yaing'ono, ndi nkhosa ziwiri;

22. ndipo padzakhala, cifukwa ca kucuruka kwa mkaka umene zidzapatsa, iye adzadya mafuta; pakuti mafuta ndi uci adzadya yense wosiyidwa pakati pa dziko.

23. Ndipo padzakhala tsiku limenelo, kuti pali ponse panali mipesa cikwi cimodzi ya mtengo wace wa ndalama cikwi cimodzi, padzakhala lunguzi ndi minga.

24. Munthu adzafikako ndi mibvi ndi uta; pakuti dziko lonse lidzakhala la lunguzi ndi minga.

25. Ndipo zitunda zonse zinalimidwa ndi khasu, iwe sudzafikako cifukwa ca kuopa lunguzi ndi minga, koma pomwepo padzakhala potumizira ng'ombe ndi popondaponda nkhosa.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 7