Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 63:13-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. amene anawatsogolera kupitira mwa kuya monga kavalo m'cipululu osapunthwa iwo?

14. Monga ng'ombe zotsikira kucigwa mzimu wa Yehova unawapumitsa; comweco inu munatsogolera anthu anu kudzitengera mbiri yaulemerero.

15. Tayang'anani kunsi, taonani pokhala panu poyera, ndi pa ulemerero wanu, cangu canu ndi nchito zanu zamphamvu ziri kuti? mwanditsekerezera zofunafuna za mtima wanu ndi cisoni canu.

16. Pakuti Inu ndinu Atate wathu, ngakhale Abrahamu satidziwa ife, ndi Israyeli satizindikira ife. Inu Yehova ndinu Atate wathu, Mombolo wathu wacikhalire ndi dzina lanu.

17. Yehova bwanji mwatisoceretsa kusiya njira zanu, ndi kuumitsa mitima yathu tisakuopeni? Bwerani, cifukwa ca atumiki anu, mafuko a colowa canu.

18. Anthu anu opatulika anakhala naco kanthawi kokha; adani athu apondereza kacisi wanu wopatulika.

19. Ife takhala ngati iwo amene simunawalamulira konse, ngati iwo amene sanachedwa dzina lanu.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 63