Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 62:10-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Pitani, pitani pazipata; konzani njira ya anthu; undani, undani khwalala; cotsani miyala, kwezani mbendera ya anthu.

11. Taonani, Yehova walalikira kufikira malekezero a dziko lapansi. Nenani kwa mwana wamkazi wa Ziyoni, Taona cipulumutso cako cifika; taona mphotho yace ali nayo, ndi nchito yace iri pamaso pace.

12. Ndipo iwo adzawacha Anthu opatulika, Oomboledwa a Yehova; ndipo iwe udzachedwa Wofunidwa, Mudzi wosasiyidwa.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 62