Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 60:16-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Iwe udzayamwanso mkaka wa amitundu, nudzayamwa bere la mafumu, nudzadziwa kuti Ine Yehova ndine mpulumutsi wako, ndi Mombolo wako, Wamphamvu wa Yakobo.

17. M'malo mwa mkuwa ndidzatenga golidi, ndi m'malo mwa citsulo ndidzatenga siliva, ndi m'malo mwa mtengo ndidzatenga mkuwa, ndi m'malo mwa miyala ndidzatenga citsulo; ndidzakuikira akapitao a mtendere, ndi oyang'anira nchito a cilungamo.

18. Ciwawa sicidzamvekanso m'dziko mwako, kupululutsa pena kupasula m'malire ako; koma udzacha malinga ako Cipulumutso, ndi zipata zako Matamando.

19. Dzuwa silidzakhalanso kuunika kwako usana, ngakhale mwezi sudzakuunikiranso kuti kuyere; koma Yehova adzakhala kwa iwe kuunika kosatha, ndi Mulungu wako adzakhala ulemerero wako.

20. Dzuwa lako silidzalowanso, mwezi wako sudzanka kumidima; pakuti Yehova adzakhala kuunika kwako kosatha, ndi masiku a kulira maliro ako adzatha.

21. Anthu ako adzakhalanso onse olungama; dzikolo lidzakhala colowa cao ku nthawi zonse, nthambi yooka Ine, nchito ya manja anga, kuti Ine ndikuzidwe.

22. Wamng'ono adzasanduka cikwi, ndi wocepa adzasanduka mtundu wamphamvu; Ine Yehova ndidzafulumiza ici m'nthawi yace.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 60