Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 6:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Caka cimene mfumu Uziya anafa, ndinaona Ambuye atakhala pa mpando wacifumu wautari, ndi wotukulidwa, ndi zobvala zace zinadzala m'Kacisi.

2. Pamwamba pa Iye panaima aserafi; yense anali ndi mapiko asanu ndi limodzi; awiri anaphimba nao nkhope yace, awiri naphimba nao mapazi ace, awiri nauluka nao.

3. Ndipo wina anapfuula kwa mnzace, nati, Woyera, Woyera, Woyera, Yehova wa makamu; dziko lonse lapansi ladzala ulemerero wace.

4. Ndipo maziko a ziundo anasunthika ndi mau amene anapfuula, ndipo nyumba inadzazidwa ndi utsi.

5. Ndipo ine ndinati, Tsoka kwa ine! cifukwa ndathedwa; cifukwa ndiri munthu wa milomo yonyansa, ndikhala pakati pa anthu a milomo yonyansa; cifukwa kuti maso anga aona Mfumu, Yehova wa makamu.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 6