Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 59:9-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Cifukwa cace ciweruziro ciri patari ndi ife, ndi cilungamo sicitipeza; tiyang'anira kuunika, koma taona mdima; tiyang'anira kuyera, koma tiyenda m'usiku.

10. Tiyambasira khoma ngati wakhungu, inde tiyambasa monga iwo opanda maso; tipunthwa usana monga m'cizirezire; tiri m'malo amdima ngati akufa.

11. Tonse tibangula ngati zirombo, ndi kulira maliro zolimba ngati nkhunda; tiyang'anira ciweruziro koma palibe; tiyang'anira cipulumutso koma ciri patari ndi ife.

12. Pakuti zolakwa zathu zacuruka pamaso pa Inu, ndipo macimo athu atineneza ife; pakuti zolakwa zathu ziri ndi ife, ndipo zoipa zathu tizidziwa;

13. ndizo kulakwabe ndi kukanabe Yehova, ndi kuleka kutsata Mulungu wathu, kulankhula zotsendereza ndi kupanduka, kuganizira ndi kunena pakamwa mau akunyenga oturuka mumtima.

14. Ndipo ciweruziro cabwerera m'mbuyo, ndi cilungamo caima patari; pakuti coona cagwa m'khwalala, ndi kuongoka sikungalowe.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 59