Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 56:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Atero Yehova, Sungani inu ciweruziro, ndi kucita cilungamo; pakuti cipulumutso canga ciri pafupi kudza, ndi cilungamo canga ciri pafupi kuti cib zumbulutsidwe,

2. Wodala munthu amene acita ici, ndi mwana wa munthu amene agwira zolimba ici, amene asunga sabata osaliipitsa, nasunga dzanja lace osacita nalo coipa ciri conse.

3. Mlendo amene wadziphatika yekha kwa Yehova asanene, kuti, Yehova adzandilekanitsa ndithu ndi anthu ace; pena mfule asanene, Taonani ine ndiri mtengo wouma.

4. Pakuti atero Yehova kwa mifule imene isunga masabata, nisankha zinthu zimene zindikondweretsa Ine, nigwira zolimba cipangano canga,

5. Kwa iyo ndidzapatsa m'nyumba yanga ndi m'kati mwa makoma anga malo, ndi dzina loposa la ana amuna ndi akazi; ndidzawapatsa dzina lacikhalire limene silidzadulidwa.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 56