Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 53:10-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Koma kunakomera Yehova kumtundudza; anammvetsa zowawa; moyo wace ukapereka nsembe yoparamula, Iye adzaona mbeu yace, adzatanimphitsa masiku ace; ndipo comkondweretsa Yehova cidzakula m'manja mwace.

11. Iye adzaona zotsatira mabvuto a moyo wace, nadzakhuta nazo; ndi nzeru zace mtumiki wanga wolungama adzalungamitsa ambiri, nadzanyamula mphulupulu zao.

12. Cifukwa cace ndidzamgawira gawo ndi akuru; ndipo adzagawana ndi amphamvu zofunkha; pakuti Iye anathira moyo wace kuimfa; ndipo anawerengedwa pamodzi ndi olakwa; koma ananyamula macimo a ambiri, napembedzera olakwa.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 53