Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 5:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndiyimbire wokondedwa wanga nyimbo ya wokondedwa wanga ya munda wace wamphesa, Wokondedwa wanga anali ndi munda wamphesa m'citunda ca zipatso zambiri;

2. ndipo iye anakumba mcerenje kuzungulira kwete, natolatola miyala pamenepo naokapo mpesa wosankhika, namangapo pakati pace nsanja, nasema mopondera mphesa, nayembekeza kuti udzabala mphesa, koma unangobala mphesa zosadya.

3. Ndipo tsopano, inu okhala m'Yerusalemu, ndi anthu a Yuda, weruzanitu mlandu wa ine ndi munda wanga wamphesa.

4. Ndikanacitanso ciani ndi munda wanga wamphesa, cimene sindinacite m'menemo; muja ndinayembekeza kuti udzabala mphesa, wabaliranji mphesa zosadya?

Werengani mutu wathunthu Yesaya 5