Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 48:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Imvani inu ici, banja la Yakobo, amene muchedwa ndi dzina la Israyeli, amene munaturuka m'madzi a Yuda amene mulumbira dzina la Yehova ndi kuchula dzina la Mulungu wa Israyeli, koma si m'zoona, pena m'cilungamo.

2. Pakuti adziyesa okha a mudzi wopatulika, ndi kudzikhazikitsa iwo okha pa Mulungu wa Israyeli; dzina lace ndi Yehova wa makamu.

3. Ndanena zinthu zoyamba kuyambira kale; inde, izo zinaturuka m'kamwa mwanga, ndipo ndinazisonyeza; mwadzidzidzi ndinazicita izo, ndipo zinaoneka.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 48