3. Marisece ako adzakhala osapfundidwa, inde, manyazi ako adzaoneka; ndidzacita kubwezera, osasamalira munthu.
4. Mombolo wathu, Yehova wa makamu ndi dzina lace, Woyera wa Israyeli.
5. Khala iwe cete, lowa mumdima, mwana wamkazi wa Akasidi; pakuti sudzachedwanso mkazi wa maufumu.
6. Ndinakwiyira anthu anga, ndinaipitsa colowa canga, ndi kuwapereka m'manja ako; koma iwe sunawaonetsera cifundo; wasenzetsa okalamba goli lako lolemera ndithu.
7. Ndipo unati, Ndidzakhala mkazi wa mfumu wa nthawi zonse; ndipo sunasamalira izi mumtima mwako, kapena kukumbukira comarizira cace.