Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 47:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Tsika, ukhale m'pfumbi, namwaliwe, mwana wamkazi wa Babulo; khala pansi popanda mpando wacifumu, mwana wamkazi wa Akasidi, pakuti iwe sudzayesedwanso wozizira ndi wololopoka.

2. Tenga mipero, nupere ufa; cotsa cophimba cako, bvula copfunda, kwinda m'mwendo, oloka mitsinje.

3. Marisece ako adzakhala osapfundidwa, inde, manyazi ako adzaoneka; ndidzacita kubwezera, osasamalira munthu.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 47