Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 46:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Beli agwada pansi, Nebo awerama; mafano ao ali pa zoweta, ndi pa ng'ombe; zinthu zimene inu munanyamula ponseponse ziyesedwa mtolo, katundu wakulemetsa nyama.

2. Milunguyo iwerama, igwada pansi pamodzi; singapulumutse katundu, koma iyo yeni yalowa m'ndende.

3. Mverani Ine, banja la Yakobo, ndi otsala onse a banja la Israyeli, amene ndakunyamulani kuyambira m'mimba, ndi kukusenzani cibadwire;

Werengani mutu wathunthu Yesaya 46