Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 45:5-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Ine ndiri Yehova, ndipo palibe winanso; popanda Ine palibe Mulungu; ndidzakumanga m'cuuno, ngakhale sunandidziwa;

6. kuti anthu akadziwe kucokera ku maturukiro a dzuwa ndi kumadzulo, kuti palibe wina popanda Ine; Ine ndine Yehova, palibe winanso.

7. Ine ndilenga kuyera ndi mdima, Ine ndilenga mtendere ndi coipa, Ine ndine Yehova wocita zinthu zonse zimenezi.

8. Igwani pansi, inu m'mwamba, kucokera kumwamba, thambo litsanulire pansi cilungamo; dziko lapansi litseguke, kuti libalitse cipulumutso, nilimeretse cilungamo cimere pamodzi; Ine Yehova ndinacilenga cimeneco.

9. Tsoka kwa iye amene akangana ndi Mlengi wace! phale mwa mapale a dziko lapansi! Kodi dongo linganene kwa iye amene aliumba, Kodi upanga ciani? pena nchito yako, Iye alibe manja?

Werengani mutu wathunthu Yesaya 45