Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 45:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Atero Yehova kwa wodzozedwa wace kwa Koresi, amene dzanja lace lamanja ndaligwiritsa, kuti agonjetse mitundu ya anthu pamaso pace, ndipo ndidzamasula m'cuuno mwa mafumu; atsegule zitseko pamaso pace, ndi zipata sizidzatsekedwa:

2. Ndidzakutsogolera ndi kusalaza pokakala; ndidzatyolatyola zitseko zamkuwa, ndi kudula pakati akapici acitsulo;

3. ndipo ndidzakupatsa iwe cuma ca mumdima, ndi zolemera zobisika za m'malo am'tseri, kuti iwe udziwe kuti Ine ndine Yehova, amene ndikuitana iwe dzina lako, ndine Mulungu wa Israyeli.

4. Ndakuitana iwe dzina lako, cifukwa ca Yakobo mtumiki wanga ndi Israyeli wosankhidwa wanga; ndakuonjezera dzina, ngakhale iwe sunandidziwa Ine.

5. Ine ndiri Yehova, ndipo palibe winanso; popanda Ine palibe Mulungu; ndidzakumanga m'cuuno, ngakhale sunandidziwa;

Werengani mutu wathunthu Yesaya 45