Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 41:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Khalani cete pamaso pa Ine, zisumbu inu, anthu atengenso mphamvu; ayandikire; pamenepo alankhule; tiyeni, tiyandikire pamodzi kuciweruziro.

2. Ndani anautsa wina wocokera kum'mawa, amene amuitana m'cilungamo, afike pa phazi lace? Iye apereka amitundu patsogolo pace, namlamuliritsa mafumu; nawapereka monga pfumbi ku lupanga lace, monga ciputu couluzidwa ku uta wace.

3. Iye awathamangitsa, napitirira mwamtendere; pa njira imene asanapitemo ndi mapazi ace.

4. Ndani wacipanga, nacimariza ico, kuchula mibadwo ciyambire? Ine Yehova, ndine woyamba, ndi pacimariziro ndine ndemwe.

5. Zisumbu zinaona niziopa; malekezero a dziko lapansi ananthunthumira; anayandikira, nafika.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 41