27. Bwanji iwe, Yakobo, umati, ndi bwanji umanena iwe, Israyeli, Njira yanga yabisika kwa Yehova; ndipo ciweruzo ca Mulungu wanga candipitirira?
28. Kodi iwe sunadziwe? kodi sunamve? Mulungu wacikhalire, Yehova, Mlengi wa malekezero a dziko lapansi, salefuka konse, salema; nzeru zace sizisanthulika.
29. Iye alimbitsa olefuka, naonjezera mphamvu iye amene alibe mphamvu.
30. Ngakhale anyamata adzalefuka ndi kulema ndi amisinkhu adzagwa ndithu:
31. koma iwo amene alindira Yehova adzatenganso mphamvu; adzauluka pamwamba ndi mapiko monga ziombankhanga; adzathamanga kuma osalema; adzayenda koma osalefuka.