Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 40:27-31 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

27. Bwanji iwe, Yakobo, umati, ndi bwanji umanena iwe, Israyeli, Njira yanga yabisika kwa Yehova; ndipo ciweruzo ca Mulungu wanga candipitirira?

28. Kodi iwe sunadziwe? kodi sunamve? Mulungu wacikhalire, Yehova, Mlengi wa malekezero a dziko lapansi, salefuka konse, salema; nzeru zace sizisanthulika.

29. Iye alimbitsa olefuka, naonjezera mphamvu iye amene alibe mphamvu.

30. Ngakhale anyamata adzalefuka ndi kulema ndi amisinkhu adzagwa ndithu:

31. koma iwo amene alindira Yehova adzatenganso mphamvu; adzauluka pamwamba ndi mapiko monga ziombankhanga; adzathamanga kuma osalema; adzayenda koma osalefuka.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 40