Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 40:24-31 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

24. Inde sanaokedwe, inde sanafesedwe; inde, muzu wao sunazike pansi; koma Iye anawaombetsera mphepo, ndipo afota, ndipo kabvumvulu awacotsa monga ciputu.

25. Mudzandifanizira Ine ndi yani tsono, kuti ndilingane naye, ati Woyerayo.

26. Kwezani maso anu kumwamba, muone amene analenga izo, amene aturutsa khamu lao ndi kuziwerenga; azicha zonse maina ao, ndi mphamvu zace zazikuru, ndi popeza ali wolimba mphamvu, palibe imodzi isoweka.

27. Bwanji iwe, Yakobo, umati, ndi bwanji umanena iwe, Israyeli, Njira yanga yabisika kwa Yehova; ndipo ciweruzo ca Mulungu wanga candipitirira?

28. Kodi iwe sunadziwe? kodi sunamve? Mulungu wacikhalire, Yehova, Mlengi wa malekezero a dziko lapansi, salefuka konse, salema; nzeru zace sizisanthulika.

29. Iye alimbitsa olefuka, naonjezera mphamvu iye amene alibe mphamvu.

30. Ngakhale anyamata adzalefuka ndi kulema ndi amisinkhu adzagwa ndithu:

31. koma iwo amene alindira Yehova adzatenganso mphamvu; adzauluka pamwamba ndi mapiko monga ziombankhanga; adzathamanga kuma osalema; adzayenda koma osalefuka.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 40