Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 40:15-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Taonani, amitundu akunga dontho la m'mtsuko, nawerengedwa ngati pfumbi losalala la m'muyeso; taonani atukula zisumbu ngati kanthu kakang'ono.

16. Ndipo Lebano sakwanira kutentha, ngakhale nyama zace sizikwanira nsembe yopsereza.

17. Amitundu onse ali cabe pamaso pa Iye; awayesa ngati cinthu cacabe, ndi copanda pace,

18. Mudzafanizira Mulungu ndi yani tsopano, kapena kumyerekeza ndi cithunzithunzi cotani?

19. Pano losema mmisiri analisungunula, ndipo wosula golidi analikuta ndi golidi, naliyengera maunyolo asiliva.

20. Wosowa nsembe yoteroyo asankha mtengo umene sungabvunde, iye adzisankhira yekha munthu mmisiri waluso, akonze fano losema, limene silisunthika.

21. Kodi inu simunadziwe? kodi inu simunamve? kodi sanakuuzani inu ciyambire? kodi inu simunadziwitse ciyambire mayambiro a dziko lapansi?

22. Ndi Iye amene akhala pamwamba pa malekerezo a dziko lapansi, ndipo okhalamo akunga ziwala; amene afutukula thambo ngati cinsaru, naliyala monga hema wakukhalamo;

23. amene asandutsa akalonga kuti akhale acabe, nasandutsa oweruza a dziko lapansi akhale opanda pace,

Werengani mutu wathunthu Yesaya 40