13. Ndinadzitonthoza kufikira mamawa; monga mkango, momwemo Iye anatyolatyola mafupa anga onse;Kuyambira usana kufikira usiku mudzanditsiriza ine.
14. Ndinalankhula-lankhula ngati namzeze, pena cumba;Ndinalira maliro ngati nkhunda;Maso anga analephera pogadamira kumwamba.Yehova ndasautsidwa, mundiperekere cikoli.
15. Kodi ndidzanena ciani?Iye wanena kwa ine, ndiponso Iye mwini wacita ici;Ine ndidzayenda cete zaka zanga zonse,Cifukwa ca zowawa za moyo wanga.
16. Ambuye ndi zinthu izi anthu akhala ndi moyo.Ndipo m'menemo monse muli moyo wa mzimu wanga;Cifukwa cace mundiciritse ine,Ndi kundikhalitsa ndi moyo.
17. Taonani, ndinali ndi zowawa zazikuru,Cifukwa ca mtendere wanga;Koma Inu mokonda moyo wanga,Munaupulumutsa m'dzanja la cibvundi,Pakuti mwaponya m'mbuyo mwanu macimo anga onse.
18. Pakuti kunsi kwa manda sikungakuyamikeni Inu;Imfa singakulemekezeni;Otsikira kudzenje sangaziyembekeze zoona zanu.
19. Wamoyo, wamoyo, iye adzakuyamikani inu, monga ine lero;Atate adzadziwitsa ana ace zoona zanu.
20. Yehova ndiye wondipulumutsa ine;Cifukwa cace tidzayimba nyimbo zanga, ndi zoyimba zazingweMasiku onse a moyo wathu m'nyumba ya Yehova.