Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 35:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Cipululu ndi malo ouma adzakondwa; ndipo dziko loti se lidzasangalala ndi kuphuka ngati duwa.

2. Lidzaphuka mocuruka ndi kusangalala, ngakhale kukondwa ndi kuyimba; lidzapatsidwa ulemerero wa Lebano, ndi ukuru wa Karimeli ndi Saroni; anthuwo adzaona ulemerero wa Yehova, ukuru wace wa Mulungu wathu.

3. Limbitsani manja opanda mphamvu, ndi kulimbitsa maondo a gwedegwede.

4. Nenani kwa a mitima ya cinthenthe, Limbani, musaope; taonani, Mulungu wanu adza ndi kubwezera cilango, ndi mphotho ya Mulungu; Iye adzafika ndi kukupulumutsani.

5. Pamenepo maso a akhungu adzatsegudwa, ndi makutu a ogontha adzatsegulidwa.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 35