Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 35:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Cipululu ndi malo ouma adzakondwa; ndipo dziko loti se lidzasangalala ndi kuphuka ngati duwa.

2. Lidzaphuka mocuruka ndi kusangalala, ngakhale kukondwa ndi kuyimba; lidzapatsidwa ulemerero wa Lebano, ndi ukuru wa Karimeli ndi Saroni; anthuwo adzaona ulemerero wa Yehova, ukuru wace wa Mulungu wathu.

3. Limbitsani manja opanda mphamvu, ndi kulimbitsa maondo a gwedegwede.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 35