3. Ophedwa aonso adzatayidwa kunja, ndipo kununkha kwa mitembo yao kudzamveka, ndipo mapiri adzasungunuka ndi mwazi wao.
4. Ndipo makamu onse a kumwamba adzasungunuka, ndi miyamba idzapindika pamodzi ngati mpukutu; makamu ao onse adzafota monga tsamba limafota pampesa ndi kugwa, ndi monga tsamba lifota pamkuyu.
5. Pakuti lupanga langa lakhuta kumwamba; taonani, lidzatsikira pa Edomu, ndi pa anthu amene ndawatemberera, kuti aweruzidwe.
6. Lupanga la Yehova lakhuta ndi mwazi, lanona ndi mafuta ndi mwazi wa ana a nkhosa, ndi mbuzi, ndi mafuta a imso ya nkhosa zamphongo; pakuti Yehova ali ndi nsembe m'Bozira, ndi ophedwa ambiri m'dziko la Edomu.
7. Ndipo njati zidzatsika ndi iwo, ndi ng'ombe zofula ndi zamphongo; ndi dziko lao lidzakhuta ndi mwazi, ndi pfumbi lao lidzanona ndi mafuta.
8. Pakuti liri tsiku la kubwezera la Yehova, caka cakubwezera cilango, mlandu wa Ziyoni.