12. Ndipo padzakhala tsiku limenelo, kuti Yehova adzaomba tirigu wace, kucokera madzi a nyanja, kufikira ku mtsinje wa Aigupto, ndipo mudzakunkhidwa mmodzi, inu ana a Israyeli.
13. Ndipo padzakhala tsiku limenelo, lipenga lalikuru lidzaombedwa; ndipo adzafika omwe akadatayika m'dziko la Asuri, ndi opitikitsidwa a m'dziko la Aigupto; ndipo adzapembedza Yehova m'phiri lopatulika la pa Yerusalemu.