Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 26:11-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Yehova, dzanja lanu litukulidwa, koma iwo saona; koma iwo adzaona cangu canu ca kwa anthu, nadzakhala ndi manyazi; inde moto udzamariza adani anu.

12. Yehova, udzatikhazikitsira mtendere; pakuti mwatigwirira nchito zathu zonse.

13. Yehova Mulungu wathu, pamodzi ndi Inu ambuye ena adatilamulira ife; koma mwa Inu nokha tidzachula dzina lanu.

14. Iwo afa, atha, sadzakhalanso ndi moyo; ali mizimu, sadzauka; cifukwa cace Inu munawazonda, ndi kuwaononga, mwathetsa cikumbukiro cao conse.

15. Mwacurukitsa mtundu, Yehova, mwacurukitsa mtundu; Inu mwalemekezeka, mwakuza malire onse a dziko.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 26