Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 25:3-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Cifukwa cace anthu amphamvu adzakulemekezani Inu, mudzi wa mitundu yakuopsya udzakuopani Inu.

4. Cifukwa Inu mwakhala linga la aumphawi, linga la osowa m'kubvutidwa kwace, pobisalira cimphepo, mthunzi wa pa dzuwa, pamene kuomba kwa akuopsya kufanana ndi cimphepo cakuomba chemba.

5. Monga kutentha m'malo ouma, Inu mudzaletsa phokoso la alendo; nyimbo ya akuopsya idzaletseka, monga mthunzi uletsa dzuwa.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 25