Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 24:17-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Mantha ndi dzenje ndi msampha ziri pa iwe, wokhala m'dziko.

18. Ndipo padzali, kuti iye amene athawa mbiri yoopsya, adzagwa m'dzenje; ndi iye amene aturuka m'kati mwa dzenje, adzakodwa mumsampha, pakuti mazenera a kuthambo atsegudwa, ndi maziko a dziko agwedezeka.

19. Dziko lapansi lasweka ndithu, dziko lapansi lasungunukadi, dziko lapansi liri kugwedezeka kopambana.

20. Dziko lapansi lidzacita dzandi dzandi, ngati munthu woledzera, ndi kunjenjemera, ngati cilindo; ndi kulakwa kwace kudzalilemera, ndipo lidzagwa losaukanso.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 24