Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 23:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Katundu wa Turo.Kuwani, inu ngalawa za Tarisi; cifukwa wapasudwa, kulibenso nyumba, kulibe polowera; kucokera ku dziko la Kitimo kwabvumbulutsidwa kwa iwo.

2. Khalani cete, inu okhala m'cisumbu; iwe amene anakudzazanso amalonda a ku Zidoni, opita m'nyanja.

3. Ndi pa nyanja zazikuru anapindula ndi mbeu za ku Sihori ndizo dzinthu za ku Nile; ndi kumeneko kunali msika wa amitundu.

4. Khala ndi manyazi, iwe Zidoni; cifukwa nyanja yanena, linga la kunyanja, ndi kuti, Ine sindinamve zowawa, kapena kubala, kapena kulera anyamata, kapena kulera anamwali.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 23