Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 23:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Katundu wa Turo.Kuwani, inu ngalawa za Tarisi; cifukwa wapasudwa, kulibenso nyumba, kulibe polowera; kucokera ku dziko la Kitimo kwabvumbulutsidwa kwa iwo.

2. Khalani cete, inu okhala m'cisumbu; iwe amene anakudzazanso amalonda a ku Zidoni, opita m'nyanja.

3. Ndi pa nyanja zazikuru anapindula ndi mbeu za ku Sihori ndizo dzinthu za ku Nile; ndi kumeneko kunali msika wa amitundu.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 23