Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 16:12-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Ndipo padzakhala kuti pamene Moabu adzadzionetsa yekha, ndi kudzitopetsa pamsanje, ndipo kufika ku malo ace oyera kudzapemphera, sadzapindulapo kanthu.

13. Awa ndi mau amene Yehova adanena za Moabu nthawi zapitazo.

14. Koma tsopano Yehova wanena, nati, Zisanapite zaka zitatu monga zaka za wolembedwa nchito, ulemerero wa Moabu udzakhala wonyozeka, ndi khamu lalikuru lace, ndi otsala adzakhala ang'ongong'ono ndi acabe.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 16