Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 14:16-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Iwo amene akuona iwe adzayang'anitsitsa iwe, nadzalingalira za iwe, ndi kuti, Kodi uyu ndi munthu amene ananthunthumiritsa dziko lapansi, amene anagwedeza maufumu;

17. amene anapululutsa dziko, napasula midzi yace, amene sanamasula ndende zace, zinke kwao?

18. Mafumu onse a amitundu, onsewo agona m'ulemerero yense kunyumba kwace.

19. Koma iwe watayidwa kunja kwa manda ako, ngati nthambi yonyansa, ngati cobvala ca ophedwa, opyozedwa ndi lupanga, otsikira ku miyala ya dzenje, monga ngati mtembo wopondedwa ndi phazi.

20. Iwe sudzaphatikizidwa pamodzi nao poikidwa, pakuti iwe waononga dziko lako, wapha anthu ako; mbeu ya ocita zoipa sidzachulidwa konse.

21. Konzani inu popherapo ana ace, cifukwa ca kuipa kwa atate ao; kuti iwo asadzauka ndi kukhala nalo dziko, ndi kudzaza dziko lapansi ndi midzi.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 14