Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 13:14-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Ndipo padzakhala kuti monga mbawala yothamangitsidwa, ndi monga nkhosa zosazisonkhanitsa anthu, adzatembenukira yense kwa anthu ace, nathawira yense ku dziko lace.

15. Onse opezedwa adzapyozedwa, ndi onse ogwidwa adzagwa ndi lupanga.

16. Makanda ao adzatswanyidwe pamaso pao; m'nyumba mwao mudzafunkhidwa, ndi akazi ao adzakakamizidwa.

17. Taonani, ndidzawautsira Amedi, amene sadzasamalira siliva, ngakhale golidi sadzakondwera naye.

18. Mauta ao adzatha anyamata; ndipo sadzacitira cisoni cipatso ca mimba; diso lao silidzaleka ana.

19. Ndipo Babulo, ulemerero wa maufumu, mudzi wokongolawo Akasidi anaunyadira, adzakhala monga momwe Mulungu anapasula Sodomu ndi Gomora.

20. Anthu sadzakhalamo konse, sadzakhalamo mbadwo ndi mbadwo; M-arabu sadzamanga hema wace pamenepo; abusa sadzagonetsa makamu ao kumeneko.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 13