Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 11:2-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. ndipo mzimu wa Yehova udzambalira iye mzimu wanzeru ndi wakuzindikira, mzimu wa uphungu ndi mphamvu, mzimu wakudziwa ndi wakuopa Yehova;

3. ndipo adzakondwera nako kumuopa Yehova, ndipo sadzaweruza monga apenya maso, sadzadzudzula mwamphekesera:

4. koma ndi cilungamo adzaweruza aumphawi, nadzadzudzulira ofatsa a m'dziko moongoka; ndipo adzamenya dziko lapansi ndi cibonga ca kukamwa kwace, nadzapha oipa ndi mpweya wa milomo yace.

5. Ndipo cilungamo cidzakhala mpango wa m'cuuno mwace, ndi cikhulupiriko cidzakhala mpango wa pa zimpsyo zace.

6. Mmbulu udzakhala pamodzi ndi mwana wa nkhosa, ndipo nyalugwe adzagona pansi ndi mwana wa mbuzi; ndipo mwana wa ng'ombe ndi mwana wa mkango ndi coweta conenepa pamodzi; ndipo mwana wamng'ono adzazitsogolera.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 11