Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 10:4-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Adzangoweramira pansi pa andende, ndipo adzagwa pansi pa ophedwa. Mwa izi zonse mkwiyo wace sunacoke, koma dzanja lace liri citambasulire.

5. Iwe Asuri cibonga ca mkwiyo wanga, ndodo m'dzanja lace muli ukali wanga!

6. Ine ndidzamtumiza kumenyana ndi mtundu wosalemekeza, ndi pa anthu a mkwiyo wanga ndidzamlangiza, kuti afunkhe, agwire zolanda, awapondereze pansi, monga dothi la pamakwalala.

7. Koma iye safuna cotero, ndipo mtima wace suganizira cotero, koma mtima wace ulikufuna kusakaza, ndi kuduladula amitundu osawerengeka.

8. Popeza ati, Akalonga anga kodi sali onse mafumu?

9. Kodi Kalino sali wonga ngati Karikemesi? kodi Hamati sali ngati Aripadi? kodi Samariya sali ngati Damasiko?

10. Popeza dzanja langa lapeza maufumu a mafano, mafano ao osema anapambana ndi iwo a ku Yerusalemu ndi ku Samariya;

11. monga ndacitira Samariya ndi mafano ace, momwemo kodi sindidzacitira Yerusalemu ndi mafano ace?

12. Cifukwa cace padzaoneka, kuti pamene Ambuye atatha nchito yace yonse pa phiri la Ziyoni ndi pa Yerusalemu, ndidzalanga zipatso za mtima wolimba wa mfumu ya Asuri, ndi ulemerero wa maso ace okwezedwa.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 10