Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 10:10-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Popeza dzanja langa lapeza maufumu a mafano, mafano ao osema anapambana ndi iwo a ku Yerusalemu ndi ku Samariya;

11. monga ndacitira Samariya ndi mafano ace, momwemo kodi sindidzacitira Yerusalemu ndi mafano ace?

12. Cifukwa cace padzaoneka, kuti pamene Ambuye atatha nchito yace yonse pa phiri la Ziyoni ndi pa Yerusalemu, ndidzalanga zipatso za mtima wolimba wa mfumu ya Asuri, ndi ulemerero wa maso ace okwezedwa.

13. Popeza anati, Mwa mphamvu ya dzanja langa ndacita ici, ndi mwa nzeru yanga; pakuti ine ndiri wocenjera; ndacotsa malekezero a anthu, ndalanda cuma cao, ndagwetsa monga munthu wolimba mtima iwo okhala pa mipando yacifumu;

14. dzanja langa lapeza monga cisa, cuma ca mitundu ya anthu, ndipo monga munthu asonkhanitsa mazira osiyidwa, ine ndasonkhanitsa dziko lonse lapansi, ndipo panalibe cogwedeza phiko, kapena cotsegula pakamwa, kapena colira pyepye.

15. Kodi nkhwangwa idzadzikweza yokha, pa iye amene adula nayo? kodi cocekera cidzadzikweza cokha pa iye amene acigwedeza, ngati cibonga ingamgwedeze iye amene ainyamula, ngati ndodo inganyamule kanthu popeza iri mtengo.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 10