Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 9:2-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. Ha, ndikadakhala ndi cigono ca anthu aulendo m'cipululu; kuti ndisiye anthu anga, ndiwacokere, pakuti onse ali acigololo msonkhano wa anthu aciwembu.

3. Ndipo apinda lilime lao ngati uta wao, liname; koma akula mphamvu m'dzikomo, koma si pacoonadi; pakuti alinkunkabe nacita zoipa, ndipo sandidziwa Ine, ati Yehova.

4. Mucenjere naye yense mnansi wace, musakhulupirire yense mbale wace; pakuti abale onse amanyenga, ndipo anansi onse adzayenda ndi maugogodi.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 9