Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 8:18-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Ha, ndikadatonthoza mtima wanga kuletsa cisoni cace! mtima wanga walefuka m'kati mwa ine.

19. Taonani, mau a kulira kwa mwana wamkazi wa anthu anga ocokera ku dziko lakutari: Kodi m'Ziyoni mulibe Yehova? Kodi mulibe Mfumu yace? Cifukwa canji andiputa Ine ndi mafano ao osema, ndi zacabe zacilendo?

20. Masika apita, mphakasa yatha, ndipo ife sitinapulumutsidwe.

21. Bala la mwana wamkazi wa anthu anga ndaphwetekwa nalo; ndada mtima; kudabwa kwandigwira.

22. Kodi mulibe bvunguti m'Gileadi? Kodi mulibe sing'anga m'menemo; analekeranji kucira mwana wamkazi wa anthu anga?

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 8