Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 8:10-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Cifukwa cace ndidzapereka akazi ao kwa ena, ndi minda yao kwa iwo adzalowamo; pakuti onse kuyambira wamng'ono kufikira wamkuru asirirasirira; kuyambira mneneri kufikira wansembe onse acita zonyenga.

11. Ndipo analipoletsa pang'ono bala la mwana wamkazi wa anthu anga, ndi kuti, Mtendere, mtendere; posakhala mtendere.

12. Kodi anakhala ndi manyazi pamene anacita zonyansa? iai, sanakhala ndi manyazi, sananyala; cifukwa cace adzagwa mwa iwo amene akugwa, nthawi ya kuyang'aniridwa kwao adzagwetsedwa, ati Yehova.

13. Kuwatha ndidzawathetsa iwo, ati Yehova, sipadzakhala mphesa pampesa, kapena nkhuyu pamkuyu, ndipo tsamba lidzafota, ndipo zinthu ndinawapatsa zidzawacokera.

14. Tikhaliranji ife? tasonkhanani, tilowe m'midzi yamalinga, tikhale cete m'menemo; pakuti Yehova Mulungu wathu watikhalitsa ife cete, natipatsa ife madzi a ndulu timwe, pakuti tamcimwira Yehova.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 8