Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 6:15-30 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Kodi anakhala ndi manyazi pamene anacita conyansa? lai, sanakhala konse ndi manyazi, sanathe kunyala; cifukwa cace adzagwa mwa iwo akugwa; panthawi pamene ndidzafika cwa iwo, aclzagwetsedwa, ati Yehova.

16. Yehova atero, Imani m'njira ndi kuona, funsani za mayendedwe akale, m'menemo muli njira yabwino, muyende m'menemo, ndipo mudzapeza mpumulo wa miyoyo yanu; koma anati, Sitidzayendamo.

17. Ndipo ndinaika alonda oyang'anira inu, ndi kuti, Mverani mau a lipenga; koma anati, Sitidzamvera.

18. Cifukwa cace tamverani, amitundu inu, dziwani, msonkhano inu, cimene ciri mwa iwo.

19. Tamva, dziko lapansi iwe; taona, Ine ndidzatengera coipa pa anthu awa, cipatso ca maganizo ao, pakuti sanamvera mau anga, kapena cilamulo canga, koma wacikana.

20. Cofukiza cindifumiranji ku Seba, ndi nzimbe ku dziko lakutari? nsembe zopsereza zanu sizindisekeretsa, nsembe zophera zanu sizindikondweretsa Ine.

21. Cifukwa cace atero Yehova, Taona, ndidzaikira anthuwa zopunthwitsa; ndipo atate ndi ana adzakhumudwa nazo pamodzi; munthu ndi mnzace adzatayika.

22. Yehova atero, Taona, mtundu wa anthu ucokera kumpoto; ndi mtundu waukuru adzaukitsidwa ku malekezero a dziko lapansi.

23. Agwira uta ndi nthungo; ali ankharwe, alibe cifundo; mau ao aphokosera ngati nyanja, akwera pa akavalo; aguba monga anthu ofuna kumenyana nkhondo ndi iwe, mwana wamkazi wa Ziyoni.

24. Tamva ife mbiri yace; manja athu alefuka, yatigwira nkhawa ndi zowawa ngati za mkazi wobala.

25. Usaturukire kumunda, usayenda m'njira; pakuti lupanga la amaliwongo ndi mantha ali m'mbali zonse.

26. Iwe mwana wamkazi wa anthu anga, udzibveke ndi ciguduli, ndi kubvimbvinika m'phulusa; ulire maliro ngati a mwana wamwamuna wa yekha, kulira kowawa koposa; pakuti wakufunkha adzatifikira ife motidzidzimutsa.

27. Ndakuyesa iwe nsanja ndi linga mwa anthu anga, kuti udziwe ndi kuyesa njira yao.

28. Onse ali opikisana ndithu, ayendayenda ndi maugogodi; ndiwo mkuwa ndi citsulo; onsewa acita mobvunda;

29. mbvukuto yatenthedwa ndi moto; mthobvu watha ndi moto wa ng'anjo; ayenga cabe; pakuti oipa sacotsedwa.

30. Anthu adzawacha nthale ya siliva, pakuti Yehova wakana iwo.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 6